16/10/2021
Mfumu Mswati ya Dziko la Eswathini, yati Anthu omwe akudana ndi ulamuliro wake ndipo akufuna ulamuliro wa Demokalase akhuta Chikokeyani ndikusuta fodya wamkulu wa Kanundu.
Mfumu Mswati wayankhula izi Ladzulori mu Mzinda wa Mbabane, M'dzikolo pa Mwambo omwe Iye amasekulira Chipatala cha Boma.
Mfumu Mswati inayankhula izi kamba ka Zionetsero zokwiya ndi ulamuliro wake zomwe zakhaka zikuchitika M'dzikolo pomwe ophunzira Sukulu akhala akunyanyala Maphunziro awo ndikuchita zionetsero Mzigawo zonse za Dzikolo.
Mfumuyi inapitilira kufotokoza kuti Anthu omwe akumatuntha Anthu kuchita zionetsero zodana ndi ulamuliro wake akumayamba alawa Ganyala pang'ono ndikukoka Ndudu ya fodya wa Kanundu akatero nkumafuna zokambirana ndi Boma lake.
Nzika za Dziko la Eswathini, Zikupitilira kuchita zionetsero zodana ndi ulamuliro wa chifumu ndipo zikunenetsa kuti tsopano yakwana nthawi yoti zikhale ndi Boma la Demokalase.
Ndine Grant Elisha Ngozo.