25/09/2025
Moni Amalawi Anzanga
Maka kwa Onse Omwe mumatsatira page lino
poyamba ndikufuna ndipeleke mafuno abwino kwa alpha peter Munthalika posankhidwa kukhala president wa dziko lino la malawi 🇲🇼
Mulungu akutsogolereni pomwe mukhale mukugwira ntchito yomwe Mulungu wakupatsani Kachikena
Amalawi zisankho zantha mpikisano uliwonse pamakhala munthu mmodzi wopambana ndipo panopa Amene mulungu wasankha ndi Amunthalika
Tiyeni tonse ngati Amalawi tigwirane Manja kuti malawi wanthuyu Apite chitsogolo
palibe munthu wina angabwele kudzatukula malawi ngati ife Eni ake sitichilimika
zilibe kanthu kuti amene wasankhidwa kukhala mtsogoleri wadziko si amene inu munamukonda dziwani kuti sizokkhumba zilizonse zomwe ife timafuna ndikukwanilitsa Ena amafa akulakalaka kudzapita dziko Lina koma maloto awo osakwanilitsidwa
Zina mulungu amazilora mwadara kuti zisachitike pa moyo wanu ndicholinga
ife tonse amene timatsatila chipani cha malawi congress tisataye mtima next time zidzayenda ndikudziwa mwaluza zinthu zochuluka ndalama zoti mukanatha kulimitsila kumunda koma zonse zapita chonde Osadzipha kapena kudzitembelera kupena kudzionera pansi nthawi ilipo zidzayenda
MALANGIZO KWA AKULUAKULU ACHIPANI CHA MCP
Dziwani kuti zinthu izi ndizomwe zatipangitsa kuti Tigonje pazisankho zangothazi
1:Kukwela kwa zinthu zofunikira Maka zipangizo za ulimi komanso zinthu Zina zofunika pamoyo wa munthu wa tsiku ndi tsiku
2:KUSAGANIZILA MOYO WA anthu ogwira ntchito m'boma pomwe zinthu zinafika povuta kukwela mitengo ya katundu Ma salale a wanthu ogwira ntchito m'boma anali Ochepa
3:KATANGALE KAPENA KUTI KUBA Kopanda nako Manyazi komangofuna zonse zikhale zanu kuiwala omwe anakuvotelani
4:IMFA YA CHILIMA NDI ANTHU ENA 8
Kaya munatengapo gawo kapena ayi izi ndichinthu chimodzi chomwe anthu sadzakuiwalani mpaka kalekale
5:KUSOWA KWA MAFUTA AGALIMOTO
munthu kuti ayende,adye ndikuchita ma business amadalira Mafuta
6:ZIPHASO ZOTULUKIRA KUNJA KOMANSO ZIPHASO ZOYENDERA PA MSEU