05/03/2024
MTSOGOLERI WA DZIKO LA ZIMBABWE KOMANSO WACHIWIRI WAKE AYIKIDWA PA CHILANGO (SANCTION) NDI DZIKO LA AMERICA.
Dziko la America lachotsa chilango chomwe chinayikidwa ku dziko la Zimbabwe ndikuyika chilangochi pa mtsogoleri wa dzikolo Emmerson Mnangagwa, komanso anthu ena kamba ka katangale komanso kuphwanya ufulu wa chibadwidwe.
Malingana ndi dziko la America, Mnangagwa amayikira kumbuyo kapena kuti kubisa anthu omwe amazembetsa miyala ya mtengo wapatali monga golide komanso kulandira ziphuphu.
Ena mwa anthu omwe ayikidwa pa chilangochi ndi mkazi wa mtsogoleri wa dziko-lo, Auxillia Mnangagwa, wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lo Constantino Chiwenga komanso nduna ya chitetezo,Oppah Muchinguri.
Ndipo dziko la America lalamula kuti katundu wa anthu omwe ayikidwa pa chilangochi, yemwe ali mdziko la America asungidwe ndi bomali.
Ndipo dziko la America lawopsezaso kuti banki ina iliyonse yomwe ipezeke ikuchita malonda ndi anthuwa, nayoso idzayikidwa pa pa chilango.
Wolemba: Alex Batison