Zina Ukava, Kamba Anga Mwala

Zina Ukava, Kamba Anga Mwala Nkhani zodabwisa,zovesa chisomo,zangochitika kumene News and events

23/05/2020



Border:

Bus ziwiri zomwe zanyamula mzika za dziko la Malawi kuchokera ku South Africa zafika pa Mwanza Border ndipo zanyamula a Malawi okwana 86, Bus Zina zokwana zisanu ndi ziwiri(7)zifika mawa la mulungu.
Anthuwo ayamba kale kuwasunga ku malo awokha wokha k*ti awunikidwe komanso ayezedwe ku kachilombo ka Corona virus, anthuwo achoka ku South Africa kamba ka mavuto omwe amakumana nawo pa nthawi ya m'bindikiro/ lockdown.

23/05/2020

*Zunews*

*MUNTHALIKA WAKWEZA PA UDINDO MAFUMU* 6*

*Mangochi*
Mtsogoleri wa dziko lino Prof Peter Munthalika wakweza pa udindo mafumu okwana 6 m'boma la Mangochi.
Mafumuwo ndi a mfumu senior Chief Chilipa, traditional Authority Ntonda, Sub traditional Authority Mambo, Mapira, Nkata ndi Namwera.
Mwambo wokweza mafumuwo anachititsa ndi nduna yowona za maboma ang'ono ang'ono Hon Ben Phiri womwe unachitikira ku Mangochi Town Hall.

22/05/2020

_*Zunews*_

BAMBO AKAKHALA KU NDENDE KWA ZAKA 7 KAMBA KOCHITA ZA MANTHANYULA NDI ANA AMUNA AWIRI



Khothi la Salima First Grade Magistrate dzana lagamula k*ti bambo Samson Kamtape a zaka 41 akakhale ku ndende kwa zaka 7 kamba kogonana ndi ana awiri a amuna kapena k*ti kuchita manthanyula, anawo ndi a zaka 9 wina wa zaka 12.
Pa 4 April 2020 bamboyo anapempha malo okhalo ku banja la ana omwe anachitidwa za manthanyulazo ndipo bamboyo anadandawula k*ti anali atangotulutsidwa kumene Kuchokera ku chipatala chachikulu Cha boma la Salima komanso anati alibe malo komwe angakagoneko, koma bamboyo nthawi zonse amakonda kupezeka ku malo omwelako mowa zomwe zinapangitsa k*ti banjalo limuthamangitse bamboyo ku nyumba yomwe anapatsidwa
Kuti azikhalamo.
Pa 6 April 2020 bamboyo anadzapitanso ku banjalo mpakana ananyengerera ana awiri a banjalo omwe ndi anyamata kuwawuza k*ti amutsatire akawapatse mankhwala ochitira ndewu ndipo anawo anamutsatira bamboyo ku malo ena komwe bamboyo anagonana nawo anawo.
Kenako bamboyo anawawopseza anawo k*ti apenga misala akawulula zomwe anawachitazo koma anawo anawulula za nkhaniyi kwa makolo awo kamba koti amkamva kupweteka kwambiri ku malo kobibila chifukwa cha manthanyulawo kenako makolowo anakanena ku polisi za nkhaniyi zomwe zinapangitsa k*ti bamboyo amangidwe.
Bambo Samson Kamtape amachokera m'mudzi mwa Machinjiri dera la mfumu Machinjiri mu mzinda wa Blantyre.

Like Zina ukanva k*t muzilandila khani zosiyana siyana komaso zina ukanva ili pa WhatsApp, +7749644719

22/05/2020

news
President Peter Mutharika has accepted the resignation by Jane Ansah.
ZUNews

22/05/2020

*_PETER KUWANI_*

*MMD* *ZUnews*

Mtsogoleri wa chipani Cha Mbakuwaku Movement For Development (MMD) a Peter Kuwani wati akadzapambana pa chisankho chachibwereza Cha pulezidenti iyeyo adzatsitsa ndalama zochitira mamphunziro ku sukulu za ukachenjede za yunivesite kufika pa Mk 150,000 pa chaka.
Iye akumakana kuchititsa misonkhano yokopa anthu kamba ka Corona virus ndipo akumakopa anthu pogwilitsa ntchito Social Media ( Facebook, WhatsApp, Radio, TV, Newspapers, ZUnews etc)

22/05/2020

_chichewa vision_🤗

*Breaking* *Zunews*

Zipani zotsutsa boma zapita ku Khothi la *Supreme Court Of Appeal* pofuna k*ti Khothi la Supreme lifotokoze momveka bwino paza yemwe akuyenera kukhazikitsa tsiku lochititsa chisankho chachibwereza Cha pulezidenti Pakati pa nyumba ya malamulo kapena bungwe la MEC.
Khumbo Soko, lawyer woyimilira wachiwiri kwa pulezidenti wa dziko lino Dr Saulos Klaus Chilima watsimikizila *ZUNEWS* za nkhaniyi ponena k*ti akufuna kudziwa Kuchokera ku Khothi za yemwe ali ndi udindo wokhazikitsa tsiku lochititsira chisankho ponena k*ti zipani zotsutsa boma sizikumvetsetsa pa nkhaniyi.
Poyamba MEC inakhazikitsa 2 July 2020 kukhala tsiku la chisankho, kenako MEC inasintha ganizo ndikunena k*ti nyumba ya malamulo ndi yomwe ikuyenera kukambilana za tsiku lochititsira chisankho koma dzulo MEC pamodzi ndi Komiti ya nyumba ya malamulo yowona za malamulo akhazikitsa 23 June 2020 kukhala tsiku lochititsira chisankho chachibwereza Cha pulezidenti.

22/05/2020

*Breaking ZUnews..*

Ku mwanza kwapezeka galimoto yomwe ak*t muli ma vote ovota vota kale

22/05/2020

*Breaking ZUnews🤔*
_*ANTHU 10 ATSOPANO APEZEKA NDI CORONA VIRUS*_

*Covid19*
Anthu 10 m'dziko muno m'mawola 24 apitawo apezeka ndi kachilombo ka Corona virus kupangitsa k*ti chiwerengero Cha anthu opezeka ndi kachilomboka chifike pa 82.
Mwa anthuwo, anthu 7 ochokera ku *Blantyre*, m'modzi ku *Phalombe* (kwathutu uku😓) m'modzi ku *Lilongwe*, m'modzi ku *Mzuzu.*
(Anthu 9 ndi mzika za dziko la Malawi pomwe m'modzi ndi mzika yaku Tanzania)
Hon Jappie Mhango nduna yaza umoyo anena izi ku Mzuzu pa msonkhano wa atolankhani.
*_MWACHIDULE_* _Anthu 82 anapezeka ndi kachilomboka, anthu 3 anamwalira pomwe anthu 27 anachila ndiye k*ti anthu 52 ndi omwe akudwala nthendayi pakadali panopo_

16/04/2020

Mwadzuka bwanji kose komwe muli , tinasowa pakatipa pazifukwa zina koma pano tabwelaso

08/10/2019
30/08/2019

Link IJA ndiimeneyo group ya pa WhatsApp

Address

Stevie From Phalombe T/A Mkhumba Gvg Nyambalo Vg Mtengo
Johannesburg
LILONGWE

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Zina Ukava, Kamba Anga Mwala posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share